Malo Ovomerezeka a pa Intaneti a Mboni za Yehova

Tsamba loyambirira Beliefs Future Medical Topics Contact Us Publications Languages

Mboni za Yehova—Kodi Iwo Ndani? Kodi Amakhulupirira Chiyani?

Nkhani yam’mbuyoNkhani yotsatira

Kodi Amakhulupirira Chiyani?

A Mboni za Yehova amakhulupirira Mulungu Wamphamvuyonse, Yehova, Mlengi wa kumwamba ndi dziko lapansi. Zinthu za chilengedwe zodabwitsa kwambiri zotizinga zimaonetsa kuti chilengedwechi chinapangidwa ndi Mlengi wanzeru ndi wamphamvu kwambiri. Monga mmene ntchito za amuna ndi akazi zimaonetsera maluso awo, zimateronso ntchito za Yehova Mulungu. Baibulo limatiuza kuti “chilengedwere dziko lapansi zaoneka bwino zosaoneka zake . . . popeza zazindikirika ndi zinthu zolengedwa.” Ndiponso, popanda mawu, “zakumwamba zimalalikira ulemerero wa Mulungu.”—Aroma 1:20; Salmo 19:1-4.

DZIKO LAPANSI . . . linalengedwa ndi Yehova . . . limasamalidwa ndi anthu . . . anthu adzakhalamo kwamuyaya

Anthu saumba mbiya kapena kupanga mawailesi akanema ndi makompyuta popanda cholinga. Dziko lapansi limodzi ndi zolengedwa zake, zomera ndi nyama n’zodabwitsa kwambiri kuposa zonsezo. Kapangidwe ka thupi la munthu limodzi ndi mamiliyoni mamiliyoni a maselo ake n’zosatheka ifeyo kuzimvetsa—ngakhale ubongo weniweniwo umene timaganiza nawo n’ngwodabwitsa moti sititha kuumvetsa! Ngati anthu amakhala ndi cholinga popanga zinthu zawo zosadabwitsa kwenikwenizo, kunena zoona Yehova Mulungu ayenera kuti anali ndi cholinga polenga zinthu zodabwitsazo! Miyambo 16:4 imati iye ali nacho cholinga mwakunena kuti: “Zonse Yehova anazipanga zili ndi zifukwa zawo.”


Yehova anali ndi cholinga popanga dziko lapansi, monga momwe anauzira anthu aŵiri oyamba kuti: “Mubalane, muchuluke, mudzaze dziko lapansi, . . . , mulamulire pa nsomba za m’nyanja, ndi pa mbalame za m’mlengalenga, ndi pa zamoyo zonse zakukwaŵa pa dziko lapansi.” (Genesis 1:28) Chifukwa chakuti anthu aŵiri oyambawo sanamvere, analephera kudzaza dziko lapansi ndi mabanja olungama amene akanasamalira bwino dziko lapansi limodzi ndi zomera ndi nyama zake. Koma kulephera kwawo sikunalepheretsenso cholinga cha Yehova. Patapita zaka zikwi zambirimbiri, olemba Mawu analemba kuti: “Mulungu amene anaumba dziko lapansi . . . , sanalilenga mwachabe.” Iye “analiumba akhalemo anthu.” Silidzawonongedwa, koma ‘dziko likhalabe masiku onse.’ (Yesaya 45:18; Mlaliki 1:4) Cholinga cha Yehova popanga dziko lapansi chidzakwaniritsidwa: “Uphungu wanga udzakhala, ndipo ndidzachita zofuna zanga zonse.”—Yesaya 46:10.

Chotero, Mboni za Yehova zimakhulupirira kuti dziko lapansi lidzakhalapo ku nthaŵi zonse ndipo anthu onse, amoyo ndi akufa, amene adzayenerera cholinga cha Yehova chokhazikitsira dziko lapansi lokongola, adzakhalapo ndi moyo kosatha. Anthu onse analandira kupanda ungwiro kuchokera kwa Adamu ndi Hava, choncho onse ndi ochimwa. (Aroma 5:12) Baibulo limatiuza kuti: “Mphoto yake ya uchimo ndi imfa.” “Amoyo adziŵa kuti tidzafa; koma akufa sadziŵa kanthu bi.” “Moyo wochimwawo ndiwo udzafa.” (Aroma 6:23; Mlaliki 9:5; Ezekieli 18:4, 20) Koma ndi motani mmene iwo angakhalirenso ndi moyo ndi kulandira nawo madalitso a m’dziko lapansi? Ndi kokha mwa nsembe ya dipo la Kristu Yesu, pakuti iye anati: “Ine ndine kuuka ndi moyo: wokhulupirira Ine, angakhale amwalira, adzakhala ndi moyo.” “Onse ali m’manda [achikumbukiro, NW] adzamva mawu ake, nadzatulukira.”—Yohane 5:28, 29; 11:25; Mateyu 20:28.

Kodi zimenezi zidzatheka motani? Zafotokozedwa mu “uthenga wabwino wa Ufumu,” umene Yesu anayamba kuulalikira pamene anali padziko lapansi. (Mateyu 4:17-23) Koma lerolino, Mboni za Yehova zikulalikira uthenga wabwino m’njira yapadera kwambiri.

ZIMENE A MBONI ZA YEHOVA AMAKHULUPIRIRA

Zimene Amakhulupirira Zifukwa za M’malemba
Baibulo ndi Mawu a Mulungu ndipo ndiwo choonadi 2 Tim. 3:16, 17; 2 Pet. 1:20, 21; Yoh. 17:17
Baibulo n’lodalirika kuposa miyambo Mat. 15:3, Akol. 2:8
Dzina la Mulungu ndi Yehova Salmo 83:18; Yes. 26:4; 42:8; Eks. 6:3
Kristu ndi Mwana wa Mulungu ndipo ndi wochepa kwa Iye Mat. 3:17; Yoh. 8:42; 14:28; 20:17; 1Akor. 11:3; 15:28
Kristu anali woyamba kulengedwa pa zolengedwa zonse za Mulungu Akol. 1:15; Chiv. 3:14
Kristu anafera pa mtengo wowongoka, osati pa mtanda Agal. 3:13; Mac. 5:30
Moyo waumunthu wa Kristu unalipiridwa monga dipo m’malo mwa anthu omvera Mat. 20:28; 1 Tim. 2:5, 6; 1 Pet. 2:24
Nsembe ya Kristu imodzi yokha inali yokwanira Aroma 6:10; Aheb. 9:25-28
Kristu anaukitsidwa kwa akufa monga munthu wauzimu wosafa 1 Pet. 3:18; Aroma 6:9; Chiv. 1:17, 18
Kukhalapo kwa Kristu kuli mwa mzimu Yoh. 14:19; Mat. 24:3; 2 Akor. 5:16; Salmo 110:1, 2
Tsopano tikukhala mu ‘nthaŵi yamapeto’ Mat. 24:3-14; 2 Tim. 3:1-5; Luka 17:26-30
Ufumu wokhala m’manja mwa Kristu udzalamulira mwa chilungamo ndi mtendere Yes. 9:6, 7; 11:1-5; Dan. 7:13, 14; Mat. 6:10
Ufumuwo udzabweretsa mikhalidwe yabwino padziko lapansi Salmo 72:1-4; Chiv. 7:9, 10, 13-17; 21:3, 4
Dziko lapansi silidzawonongedwa kapena kukhala lopanda anthu Mlal. 1:4; Yes. 45:18; Salmo 78:69
Mulungu adzachotsa maulamuliro amene alipoŵa pankhondo ya Armagedo Chiv. 16:14, 16; Zef. 3:8; Dan. 2:44; Yes. 34:2; 55:10, 11
Oipa adzawonongedwa ndi kusadzakhalakonso Mat. 25:41-46; 2 Ates. 1:6-9
Anthu oyanjidwa ndi Mulungu adzalandira moyo wosatha Yoh. 3:16; 10:27, 28; 17:3; Marko 10:29, 30
Pali njira imodzi yokha ya ku moyo Mat. 7:13, 14; Aef. 4:4, 5
Imfa ya anthu inadza ndi tchimo la Adamu Aroma 5:12; 6:23
Munthu yense pamodzi ndi mzimu wake amathera pa imfa Ezek. 18:4; Mlal. 9:10; Salmo 6:5; 146:4; Yoh. 11:11-14
Helo ndi manda a anthu onse Yobu 14:13; Chiv. 20:13, 14
Chiyembekezo cha akufa n’cha kuukitsidwa 1 Akor. 15:20-22; Yoh. 5:28, 29; 11:25, 26
Imfa ya kwa Adamu idzatha 1 Akor. 15:26, 54; Chiv. 21:4; Yes. 25:8
Kagulu kankhosa 144,000 zokha ndiko kakupita kumwamba kukalamulira limodzi ndi Kristu Luka 12:32; Chiv. 14:1, 3; 1 Akor. 15:40-53; Chiv. 5:9, 10
A m’gulu la 144,000 amabadwanso monga ana a Mulungu auzimu 1 Pet. 1:23; Yoh. 3:3; Chiv. 7:3, 4
Pangano latsopano limapangidwa ndi Israyeli wauzimu Yer. 31:31; Aheb. 8:10-13
Mpingo wa Kristu unamangidwa pa iyemwini Aef. 2:20; Yes. 28:16; Mat. 21:42
Mapemphero ayenera kuperekedwa kwa Yehova yekha kudzera mwa Kristu Yoh. 14:6, 13, 14; 1 Tim. 2:5
Mafano sayenera kugwiritsidwa ntchito polambira Eks. 20:4, 5; Lev. 26:1; 1 Akor. 10:14; Salmo 115:4-8
Kukhulupirira zamizimu kuyenera kupeŵedwa Deut. 18:10-12; Agal. 5:19-21; Lev. 19:31
Satana ndiye wolamulira dziko wosaoneka 1 Yoh. 5:19; 2 Akor. 4:4; Yoh. 12:31
Mkristu sayenera kukhala m’mabungwe ophatikiza zipembedzo zosiyanasiyana 2 Akor. 6:14-17; 11:13-15; Agal. 5:9; Deut. 7:1-5
Mkristu ayenera kulekana ndi dziko Yak. 4:4; 1 Yoh. 2:15; Yoh. 15:19; 17:16
Malamulo onse a anthu amene sawombana ndi malamulo a Mulungu tiyenera kuwamvera Mat. 22:20, 21; 1 Pet. 2:12; 4:15
Kuloŵetsa magazi m’thupi kudzera m’kamwa kapena m’mitsempha ndi kuphwanya malamulo a Mulungu Gen. 9:3, 4; Lev. 17:14; Mac. 15:28, 29
Malamulo a m’Baibulo onena za makhalidwe abwino tiyenera kuwatsatira 1 Akor. 6:9, 10; Aheb. 13:4; 1 Tim. 3:2; Miy. 5:1-23
Lamulo losunga Sabata linaperekedwa kwa Aisrayeli okha ndipo linatha limodzi ndi Chilamulo cha Mose Deut. 5:15; Eks. 31:13; Aroma 10:4; Agal. 4:9, 10; Akol. 2:16, 17
Kukhala ndi gulu lapamwamba la atsogoleri achipembedzo ndi mayina apamwamba aulemu wapadera n’kosayenera Mat. 23:8-12; 20:25-27; Yobu 32:21, 22
Munthu sanachite kusinthika koma anachita kulengedwa Yes. 45:12; Gen. 1:27; Mat. 19:4
Kristu anapereka chitsanzo chimene tiyenera kutengera potumikira Mulungu 1 Pet. 2:21; Aheb. 10:7; Yoh. 4:34; 6:38
Ubatizo womiza thupi lonse m’madzi ndi chizindikiro cha kudzipatulira Marko 1:9, 10; Yoh. 3:23; Mac. 19:4, 5
Akristu amasangalala popereka poyera umboni wa choonadi cha m’Malemba Aroma 10:10; Aheb. 13:15; Yes. 43:10-12
 

Kofalitsidwa mu 2000

Tsamba loyambiriraPamwambaNkhani yam’mbuyoNkhani yotsatira